Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amumanga atanamiza anthu kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga

Apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre amanga Rodrick Kaliwo wazaka 28 pomuganizira kuti wakhala akubera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga.

Kaliwo anamangidwaponso pamulandu ngati womwewu.

Ofalitsankhani wapolisi ku Limbe, Aubrey Singanyama, wati Kaliwo anatenga ndalama yokwana K60,000 kwa munthu wina wa bizinesi pomunamiza kuti adzayichulukitsa kukwana K900,000 mmaola awiri okha.

Zitakanika, mkuluyu anauza munthu wabizinesiyo kuti akatenge dothi la mtumbira wa manda omwe angokwiliridwa kumene, zomwe zinamudabwitsa kenako anakanena kupolisi.

Apolisi atafika kunyumba kwa Kaliwo, anapeza zinthu zosiyanasiyana zomwe amanamizira anthu kuti iyeyo ndi sing’anga.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

A Bango ayamika Dr Chakwera chifukwa choganizira anthu a m’boma la Kasungu

Mayeso Chikhadzula

Nzika ya Niger akuyisunga ku Maula

Romeo Umali

Govt calls for sanity on gold panning in Zomba

Kumbukani Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.