Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amumanga atanamiza anthu kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga

Apolisi ku Limbe munzinda wa Blantyre amanga Rodrick Kaliwo wazaka 28 pomuganizira kuti wakhala akubera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga.

Kaliwo anamangidwaponso pamulandu ngati womwewu.

Ofalitsankhani wapolisi ku Limbe, Aubrey Singanyama, wati Kaliwo anatenga ndalama yokwana K60,000 kwa munthu wina wa bizinesi pomunamiza kuti adzayichulukitsa kukwana K900,000 mmaola awiri okha.

Zitakanika, mkuluyu anauza munthu wabizinesiyo kuti akatenge dothi la mtumbira wa manda omwe angokwiliridwa kumene, zomwe zinamudabwitsa kenako anakanena kupolisi.

Apolisi atafika kunyumba kwa Kaliwo, anapeza zinthu zosiyanasiyana zomwe amanamizira anthu kuti iyeyo ndi sing’anga.

Related posts

Malawi, Uganda and Kenya holding talks on ending child labor

Romeo Umali

SCT gives hope to Cyclone Freddy survivors in Nsanje

MBC Online

Flames yakale isewera ndi Zambia yakale

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.