Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Malawi ali ndi kuthekera kochita bwino payekha’

Katswiri olemba mabuku otchedwa Blessings Chiwosi wati pali zinthu zambiri zomwe dziko la Malawi lingathe kuchita kuti lipite chitsogolo pazachuma komanso chitukuko.

Chiwosi wanena izi pambuyo po kukhazikitsa bukhu lomwe walemba lotchedwa “Malawian wealth creation” lomwe akutambasulamo zinthu zomwe dziko lino likuyenera kuchita kuti likhale lodziyimira palokha.

Mwazina bukhuli lafotokozapo zaulimi komanso nkhani za malonda ndi kuika chidwi pa ntchito zaluso. Iye wati ndizotheka dziko la Malawi kudzichotsa lokha paumphawi koma wati zitengera atsogoleri kugwiritsa ntchito ukadaulo omwe waulemba m’bukuli.

M’mawu ake mkulu wa zamapulani a dziko, a Thomas Munthali ati ndiokondwa kuti achinyamata akuikapo chidwi pokwanitsa masomphenya a dziko. Iwo ati kulemba bukhu logwirizana ndi masomphenyawa ndichitsimikizo choti achinyamata sanatsalire m’mbuyo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bullets suspend Kajoke

MBC Online

Mzimba Stadium yatsala pang’ono kutha

Justin Mkweu

Gogo Karonga laid to rest, VP and Muluzi attend funeral

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.