Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ophunzira pa UNIMA akhazikitsa kampani ya luso lamakono

Ophunzira pa sukulu yaukachenjede ya University of Malawi(Unima) ku Zomba akhazikitsa chipangizo chothandiza anthu omwe ali ndi ulumali wosaona.

Mmodzi mwa ophunzirawo, Hudson Mwangalika, wati mwa zina, chipangizocho, chomwe amavala ku maso ngati magalasi, chimatulutsa phokoso yemwe wachivalayo akayandikira chinthu kutsogolo kwake. Izi zimathandiza kuti munthuyo asaombane ndi chinthucho.

Izi zadziwika pomwe ophunzirawo amakhazikitsa kampani yawo ya luso lamakono yotchedwa HB Space TL.

Pamwambowo, ophunzirawo anawonetsanso chipangizo chotayiramo zinyalala chotchedwa smart bin chomwe chimatseguka chokha mkati mwake munthu akachiyandikira komanso kuchibaibitsa. Ophunzirawo anawonetsanso zipangizo zina za luso lamakono.

Ndipo m’mau ake, mkulu oona za luso la makono mu unduna wa za maphunziro, Chomora Mikeka, wati zomwe achinyamatawa akonza, zingathandize kuchepetsa ndalama zomwe dziko lino limaononga pogula zipangizo ngati zomwezi kuchokera ku maiko akunja.

Related posts

Govt affirms commitment to resolving water challenges in Dowa

Rabson Kondowe

Dr Chilima anali wosayang’ana zigawo – Kaliati

Alinafe Mlamba

New Anti-Money Laundering Policy launched

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.