Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Ofesi ya khonsolo ya Mangochi yatsopano idzathandiza koposa’

Ntchito yomanga ofesi ya tsopano ya khonsolo ya Mangochi akuti ithandiza kwambiri m’mene adindo amagwilira ntchito.

Izi zili chomwechi kaamba koti adindo anthambi zambiri zofunikira adzigwira ntchito pamalo amodzi kusiyana ndi mmene zinthu zilili pano pamene ofesi zili mbali ina ya town ya Mangochi.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, masanawa anayendera ntchito yomanga ofesiyi ndipo anabzyalapo mtengo.

Pakadali pano, Dr Chakwera ndi Mayi Monica Chakwera anyamuka ulendo opita kukayendera ntchito yomanga msewu wa Monkey Bay – Cape Maclear.

Olemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHAKWERA HOMEBOUND

MBC Online

Dr Usi attends Thanksgiving, farewell mass

Beatrice Mwape

Chipatala cha Namatumi ku Thyolo achimaliza kumanga

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.