Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Ofesi ya khonsolo ya Mangochi yatsopano idzathandiza koposa’

Ntchito yomanga ofesi ya tsopano ya khonsolo ya Mangochi akuti ithandiza kwambiri m’mene adindo amagwilira ntchito.

Izi zili chomwechi kaamba koti adindo anthambi zambiri zofunikira adzigwira ntchito pamalo amodzi kusiyana ndi mmene zinthu zilili pano pamene ofesi zili mbali ina ya town ya Mangochi.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, masanawa anayendera ntchito yomanga ofesiyi ndipo anabzyalapo mtengo.

Pakadali pano, Dr Chakwera ndi Mayi Monica Chakwera anyamuka ulendo opita kukayendera ntchito yomanga msewu wa Monkey Bay – Cape Maclear.

Olemba: Owen Mavula

Related posts

UK doctor takes breast cancer fight to Thyolo

MBC Online

‘Demanding fees from patients is illegal’

Romeo Umali

The Harps ikondwerera zaka khumi zamaimbidwe ndi makwaya aku Zimbabwe ndi Zambia

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.