Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

“Ndabwela kudzagwira ntchito” — Uladi Mussa

Yemwe anali wachiwiri kwa prezidenti wachipani cha Democratic Progressive Party (DPP), a Uladi Mussa, wati agwira ntchito limodzi ndi atsogoleli achipani cha MCP pofuna kuonetsetsa kuti chipanichi chipitilire kukhala champhamvu.

A Mussa amayankhula ku Dedza pabwalo la Phillip Holseman kumene mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera amachititsa msonkhano wa chitukuko.

Mwa zina a Mussa ati ma area omwe adawakhazikitsa okwana 188 tsopano awasandutsa kukhala a chipani cha MCP.

Iwo adalowa m’chipani cha MCP masiku apitawa kuchoka kuchipani cha DPP ati poona mfundo zabwino zomwe mtsogoleri wa dziko lino akutsatila potsogolela dziko lino.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

MACODA launch disability act booklet

MBC Online

Chakwera leaves Namibia

Chiyembekezo Kapatamoyo

A budget of hope and optimism

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.