Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mwala otayidwa unasanduka mwala wapangodya, watero Msonda

A Ken Msonda, omwe alandiridwa ku chipani cha Malawi Congress MCP dzulo, ati ndi odabwitsidwa ndi chilimbikitso chimene apatsidwa ndi mafumu akuluakulu a m’boma la Rumphi pamene alowa m’chipanichi.

Iwo ati sizinachitikepo mu mbiri ya ndale m’dziko muno mafumu kuperekeza munthu kukalowa chipani.

Polowa m’chipani cha MCP, a Ken Msonda anaperekezedwa ndi mafumu motsogozedwa ndi Paramount Chief Chikulamayembe komanso m’busa Victor Chikhosa wa mpingo wa Chiweta CCAP, mwa ena.

“Ambuye watseka pakamwa onse wotukwana, wolalata, wonyoza,” atero a Msonda.

By Blessings Cheleuka

Related posts

Kanema wa Justice amuonetsa dziko lonse

Romeo Umali

Salima Sugar ikupereka K500 million kwa osamuka m’minda yawo

Romeo Umali

Bungwe la FAO lithandiza dziko la Malawi

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.