Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Musapereke za unzika kwa aliyense — Kunkuyu

Boma ladzudzula m’chitidwe omwe anthu ena akumachita otenga ziphaso za unzika za anthu ena powanamiza kuti awamangira nyumba, mwa zina.

Nduna yofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, atsindikiza izi lero mu mzinda wa Blantyre komwe anati boma likhazikitsa zilango zokhwima zomwe zidzagwire ntchito kwa aliyense opezeka olakwa.

Iwo ati m’chitidwewu ndi osavomerezeka ndipo aMalawi akhale tcheru ndikukaneneza ku Polisi onse amene akuchita izi.

Olemba: Timothy Kateta

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Madam Chakwera dates TB, Leprosy survivors

Beatrice Mwape

CHAM donates motorcycles to health facilities

Alinafe Mlamba

Tigwirane manja potolera ndalama zoyendetsera ligi — SULOM

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.