Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Muli ndi ufulu olowa chipani chomwe mwafuna – Brown Mpinganjira

Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha Malawi Congress Party (MCP) m’chigawo chakum’mwera, a Brown Mpinganjira, apempha anthu a m’boma la Thyolo kuti asamaope kapena kuopsezedwa ndi anthu a zipani zina akafuna kulowa chipani cha MCP.

A Mpinganjira amayankhula izi kwa Bvumbwe m’bomali pamene amapereka zovala za makaka a chipani cha MCP monga ma T-Shirt ndi nsalu.

Iwo anapitirizanso kunena kuti dziko la Malawi ndi lazipani zambiri ndipo anthu ali ndi ufulu olowa chipani chomwe angafune.

A Mpinganjira apemphanso anthu kuti adzavotere  aphungu a MCP mu chisankho cha mchaka cha 2025.

 

 

By Alufisha Fischer.

Related posts

K540 million loan initiative empowers communities in Chitipa

Rabson Kondowe

Malawi Beach Soccer National Team promises fireworks in AFCON Beach Soccer Qualifier

Romeo Umali

Govt commits to improve children’s welfare

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.