Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Muli ndi ufulu olowa chipani chomwe mwafuna – Brown Mpinganjira

Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha Malawi Congress Party (MCP) m’chigawo chakum’mwera, a Brown Mpinganjira, apempha anthu a m’boma la Thyolo kuti asamaope kapena kuopsezedwa ndi anthu a zipani zina akafuna kulowa chipani cha MCP.

A Mpinganjira amayankhula izi kwa Bvumbwe m’bomali pamene amapereka zovala za makaka a chipani cha MCP monga ma T-Shirt ndi nsalu.

Iwo anapitirizanso kunena kuti dziko la Malawi ndi lazipani zambiri ndipo anthu ali ndi ufulu olowa chipani chomwe angafune.

A Mpinganjira apemphanso anthu kuti adzavotere  aphungu a MCP mu chisankho cha mchaka cha 2025.

 

 

By Alufisha Fischer.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MUKADALITSA HITS 61,000 VIEWS IN JUST 6 HOURS!

Alinafe Mlamba

Maeresa retires from MBC

Government steadfast in promoting youth empowerment

Davie Umar
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.