Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Mnyamata wazaka 18 wapambana ku Misuku

Hope Msukwa, amene ndi wa zaka 18, wapambana pa mpikisano okwera njinga zamoto kumapiri aku Misuku m’boma la Chitipa.

Iyeyu wapambana atayendetsa njinga yamoto kwa mphindi 47 pa mtunda wama kilometre 48 ndipo wapeza mphoto ya K1.4 million komanso wagonjetsa anyamata ena oposa 49 amene amapikisana nawo.

Hope anati agwiritsa ntchito ndalamayo kuti agule njinga yake chifukwa imene amagwiritsa ntchito pa mpikisanowo ndi yobwereka.

Thokozani Kanyika ndi amene wakhala wachiwiri ndipo walandira K900,000 pamene Zakaria Kaini wathera pachitatu ndipo walandira K615,000.

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

Phalombe District Forum donates assorted items to Reverend John Chilembwe Hospital

Rabson Kondowe

Financial institutions urge construction players to explore funding opportunities

Romeo Umali

Tobacco rakes in $53.7 million

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.