Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Malawi Fertilizer Company itha kupanga fertilizer okwana 150, 000 tons

Mkulu wa fakitole ya Malawi Fertilizer Company, a Christopher Keen, ati ili ndi kuthekera kopanga ma tani okwana 150, 000 a feteleza pa chaka.

A Keen amayankhula kwa alimi oposa 100 a minda ikuluikulu amene amayendera kampaniyi ku Liwonde kuti apeze mwayi odziwa m’mene feteleza amagwirira ntchito mu nthaka komanso kudziwa feteleza oyenera pamunda wawo kuti akolole zochuluka.

M’modzi mwa alimiwa, a Jonathan Kamakanda, anati chiyambire ntchito ya minda ikuluikulu, iwo akupeza phindu.

Iwo anati izi zili chomwechi chifukwa boma layika njira zabwino zobweretsera pamodzi akatswiri pa zaulimi m’magawo ambiri amene akuwathandiza kudziwa bwino za feteleza ndi nthaka.

Oyang’anira ntchito ya minda ikuluikulu ku unduna wa zaulimi, a MacDonald Chikhawo, anati ntchito yawo ndi alimi ena ikuonetsa tsogolo labwino kaamba koti nthambi zonse zokhudzidwa ndi ulimi zikuonetsa chidwi chothandiza alimi kutukuka monga mwa masomphenya a Malawi a 2063.

Related posts

Sendeza ayendera Hope Orphanage

Yamikani Simtowe

‘Tisunge bata’

Mayeso Chikhadzula

NEEF yakhazikitsa ngongole ya ulimi wa mthilira

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.