Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Kuphunzira m’magulu kuli ndi phindu

Mlangizi wa zamaphunziro ku Zone ya Kabuthu ku Lilongwe, a Efrida Ndau, walimbikitsa aphunzitsi a msukulu za primary m’dziko muno kuphunzitsa ophunzira awo m’magulu.

Malinga ndi a Ndau, kuphunzitsa mwamtunduwu kumathandiza kuti ophunzira adzikhala ndi chidwi pamaphunziro komanso kugawana nzeru mosavuta.

A Ndau anena izi pomwe mtsogoleri wa bungwe la Japanese International Corporation Agency (JICA), a AkihikoTanaka, anayendera zina mwantchito za maphunziro zomwe zili pansi pabungweli mderali.

A Tanaka ayamikira ubale omwe ulipo pakati pa aphunzitsi am’dziko muno, ophunzira komanso aphunzitsi omwe anachoka ku dziko la Japan kudzagwira ntchito yophunzitsa msukulu za primary m’dziko muno modzipereka.

Related posts

FOMO in a ‘precarious’ position

Romeo Umali

Malawi conducts first study on Parkinson’s Disease

Romeo Umali

Chakwera calls for continued support to boost Malawi’s food security

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.