Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Development Local Local News

Lamulo ligwira ntchito tikakupezani mukuzembetsa fodya — Boma

Boma, kudzera ku unduna oona za ulimi m’dziko muno, lachenjeza alimi komanso a Malawi kuti kuzembetsa fodya ndi kukamugulitsa m’maiko ena ndi kusakonda dziko lino.

A Geoffrey Mamba, amene ndi mlembi ku undunawu, ndi wapereka chenjezoli pamene amatsegulira msika wa fodya mu mzinda wa Mzuzu.

Iwo ananenetsa kuti lamulo lidzagwira ntchito kwa onse amene adzawapeze akuchita m’chitidwe wa chinyengowu.

“Fodya ndi mbewu yotetezedwa ndipo sitingalore kuti anthu ena atibere phindu lathu,” a Mamba anafotokoza.

Alimi amene MBC Digital yayankhula nawo ku Mzuzuko aonetsa kukondwa kaamba ka mitengo yomwe ogula akupereka, popeza mitengo yomwe ogula akupereka pa fodya wa contract ndi $3.15 komanso $2.99.

Olemba: George Mkandawire

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Boma, asodzi agwirana manja pofuna kuchulukitsa nsomba m’nyanja ya Malawi

Beatrice Mwape

Apereka chindapusa pa milandu yosakaza chilengedwe

Mayeso Chikhadzula

First MDF female pilot to be buried in Thyolo

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.