Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chakwera wanyamuka kubwelera ku Lilongwe

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, wanyamuka m’chigawo chakummwera, kudzera pa bwalo la ndege la Chileka, kubwelera ku Lilongwe.

A Chakwera anali m’chigawo chakummwera pa Limbe Police Training School mumzinda wa Blantyre, kumene anatsogolera mwambo otulutsa apolisi omwe atsiriza maphunziro awo.

Nduna ya zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, nduna yoona za madzi ndi ukhondo, a Abida Mia, mafumu komanso atsogoleri andale ndi ena mwa anthu omwe anatsanzikana ndi Dr Chakwera komanso Madam Monica Chakwera pabwalo la ndege la Chileka.

Related posts

Khothi laimitsa kaye mlandu wa mmwenye ndi mavenda aku Nsungwi

Mayeso Chikhadzula

‘Thetsani nkhanza kwa anthu achialubino’

Romeo Umali

Alimi ndi okhutira ndi kampani zogula fodya

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.