Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chakwera wanyamuka kubwelera ku Lilongwe

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, wanyamuka m’chigawo chakummwera, kudzera pa bwalo la ndege la Chileka, kubwelera ku Lilongwe.

A Chakwera anali m’chigawo chakummwera pa Limbe Police Training School mumzinda wa Blantyre, kumene anatsogolera mwambo otulutsa apolisi omwe atsiriza maphunziro awo.

Nduna ya zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, nduna yoona za madzi ndi ukhondo, a Abida Mia, mafumu komanso atsogoleri andale ndi ena mwa anthu omwe anatsanzikana ndi Dr Chakwera komanso Madam Monica Chakwera pabwalo la ndege la Chileka.

Related posts

‘Anthu opitilira 3,000 amwalira kaamba ka vuto la mpima’

Rabson Kondowe

Mkazi wa malemu Professor Mumba amupeza wolakwa pa mlandu wokupha

Mayeso Chikhadzula

Apolisi agwira mbala zomwe zinaba katundu wa Radio Maria

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.