Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani Sports

K80.4 million yapezeka pamasewero a Bullets ndi Wanderers

Ndalama zokwana K80.4 million ndi zomwe zapezeka pa masewero amu ligi ya TNM apakati pa matimu a FCB Nyasa Big Bullets komanso Mighty Mukuru Wanderers omwe aseweredwa loweruka masana pabwalo la Kamuzu.

Matimu a Wanderers komanso Bullets atenga K16.7 million timu iliyonse kuchoka pa ndalamayi (K80.4 million)

Chaka chatha, pamasewero ngati omwewa ndalama pafupifupi K67.5 million ndi zomwe zinapezeka.

Masewerowa athera 1-1 pomwe Wanderers inagoletsa kudzera mwa Isaac Kaliati ndipo Bullets inagoletsa kudzera mwa Patrick Mwaungulu.

Wolemba Praise Majawa.

Related posts

When plastic blocks drains, disaster strikes

Romeo Umali

Parliament to hold open session in Dedza

Romeo Umali

Farmers benefit from financial inclusion project

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.