Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Gawo lachitatu la kalembera wazisankho wayamba

Wapampando wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), a Justice Annabel Mtalimanja, wapempha aMalawi kuti achotse chikayiko chimene angakhale nacho pa makina amakono akalembera wamavoti.

A Mtalimanja anena izi pamene gawo lachitatu lakalembera wa m’kaundula wachisankho wayamba m’madera ena a m’maboma a Lilongwe, Mchinji, Mangochi, Chikhwawa, Nsanje ndi Mzimba.

Iwo anatu, “anthu ena akuganiza kuti makinawa ndi ovotera kapena kubera zisankho, ayi. Taonani sipanathe mphindi ziwiri ine ndalembetsa.”

Wapampandoyu anapemphanso zipani za ndale kuti zikhale patsogolo kuwunikira anthu zokhudza ubwino olembetsa m’kaundulayu.

 

Related posts

Parliamentarians call for action on agriculture development at Accra meeting

McDonald Chiwayula

Voting commences in the UTM elective convention

MBC Online

MEC Commissioner impressed with Balaka

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.