Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Gawo lachitatu la kalembera wazisankho wayamba

Wapampando wa bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), a Justice Annabel Mtalimanja, wapempha aMalawi kuti achotse chikayiko chimene angakhale nacho pa makina amakono akalembera wamavoti.

A Mtalimanja anena izi pamene gawo lachitatu lakalembera wa m’kaundula wachisankho wayamba m’madera ena a m’maboma a Lilongwe, Mchinji, Mangochi, Chikhwawa, Nsanje ndi Mzimba.

Iwo anatu, “anthu ena akuganiza kuti makinawa ndi ovotera kapena kubera zisankho, ayi. Taonani sipanathe mphindi ziwiri ine ndalembetsa.”

Wapampandoyu anapemphanso zipani za ndale kuti zikhale patsogolo kuwunikira anthu zokhudza ubwino olembetsa m’kaundulayu.

 

Related posts

Bishop Mtumbuka launches football tourney for peace

Rabson Kondowe

Mzuzu tobacco market opens, farmers satisfied with prices

Rabson Kondowe

Three sentenced to 12 years imprisonment for robbery with violence

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.