Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Dr Chilima anathandiza nawo pomenyera ufulu wa democracy — Silungwe

A Chikosa Silungwe, omwe anali nzawo wa malemu Dr Saulos Chilima, ati malemu Dr Chilima anathandiza kumenyera kuti m’dziko muno mubwere ulamuliro wa zipani zambiri (multiparty democracy).

A Silungwe ati Dr. Chilima anapanga zimenezi mogwirizana ndi anzawo ambiri amene pa nthawiyo anali msukulu zosiyanasiyana za ukachenjede.

A Silungwe atinso Dr. Chilima anali munthu wa nzeru, wamsangala kwambiri ndipo kuli konse komwe adagwira ntchito amasiya mbiri yabwino.

Pothilira ndemanga pa ntchito za boma, iwo anati Dr. Chilima amaonetsa chitsanzo monga kusunga nthawi komanso kudzipereka kwathunthu pogwira ntchito iliyonse.

A Silungwe agwirizana ndi akubanja la a Chilima kupempha boma kuti pachitike kafukufuku wokwanira pa ngozi imene yadzetsa imfayi.

 

Olemba: Isaac Jali

Related posts

MPS REBUKES LONGWE, ASSURES CITIZENS OF SECURITY

MBC Online

‘Mtayakhasu ndi ulimi othana ndi njala’

Romeo Umali

FOMO in a ‘precarious’ position

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.