Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

Dr. Chakwera wapepesa a Katolika pa imfa ya Papa

Prezidenti wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera ndi Mayi wa dziko lino, Madam Monica Chakwera, ati ndi okhudzika kwambiri ndi imfa ya mtsogoleri wa mpingo wa Katolika pa dziko lonse, Papa Francis.
Chikalata chomwe atulutsa, Dr. Chakwera wati anali ndi mwayi okumana ndi mtsogoleriyu miyezi isanu ndi inayi yapitayi ndipo wati Papa Francis wasiya mbiri yabwino yolimbikitsa chikhulupiliro,chikondi, kudzipereka komanso kulimbikitsa mtendere,chilungamo ndi umodzi.
Prezidenti Chakwera wati Papa Francis adzakumbukiridwa pa chidwi chake cholimbikitsa utsogoleri wabwino, omwe iye anali chitsanzo posintha mayendetsedwe a mpingo wa Katolika mu njira zosiyanasiyana.
Apa Dr.Chakwera ndi Madam Monica Chakwera apepesa akubanja la Papa Francis, akhristu a mpingo wa Katolika kuno ku Malawi ndi dziko lonse pa Imfayi.

Related posts

First-round crop estimates show slight increase in maize production

Rabson Kondowe

Four die in Lingadzi road accident

Romeo Umali

Education ministry eyes ODeL expansion as learner numbers rise

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.