Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Development Local Local News Nkhani

Alimi ndi okhutira ndi kampani zogula fodya

Alimi a fodya a m’maboma a Kasungu ndi Dowa ati ndi okhutira ndi kuchuluka kwa kampani zogula fodya pa msika omwe watsegulira lero mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

Ena mwa alimiwa ati fodya wa kontalakiti komanso auction akumugula pa mitengo ya bwino kwambiri kusiyana ndi zaka zam’mbuyomo.

Iwo ati akugulitsa fodya wawo wa kontalakiti pansi pa kampani za Nyasa Tobacco, JTI ndi Alliance One, mwa ena.

Pomwe amatsekulira msika wa fodya wa chaka chino ku Chinkhoma m’boma la Kasungu, fodya amamugula pa mtengo wa $3.01 ndipo wotsika amafika pa $2.55.

Mabelo wokwana 2, 165 ndi omwe awagulitsa koma msikawu umatha kugulitsa mabelo 7,000 patsiku.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Chiganizo chotuluka mu mgwirizano tidzatsimikiza pa 19 July — UTM

Romeo Umali

Gender Mainstream drill to improve fight against GBV — Yolamu

Alinafe Mlamba

Flames should develop from U-20 ranks — Analysts

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.