Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Bullets isewera nawo mu mpikisano wa CAF

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yati itenga nawo mbali mumpikisano wa CAF Champions League chaka chino.

Izi zikudza pamene pakhala pali mtsutso pakati pa otsatira masewero ampira wamiyendo ngati ndi koyenera kuti timuyi itenge nawo gawo mumpikisanowu kapena wa Confederation Cup.

Mmodzi mwa akuluakulu a Bullets, Albert Chigoga, wati apereka kalata zofunikira zonse zoonetsa chidwi chawo choti atenge nawo gawo mumpikisanowu chaka chino ku bungwe la Football Association of Malawi.

Chigoga wati agwiritsa ntchito ndalama zambiri mumpikisanowu ngakhale akana kunena mlingo wa ndalamazo.

Bungwe la Football Association of Malawi posachedwapa lidalengeza kuti lidzithandiza matimu omwe adzitenga nawo gawo muchikho cha CAF.

Related posts

Bungwe la Red Cross lapereka ndalama kwa mabanja okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi

Rabson Kondowe

Chakwera ndi chiyembekezo cha dziko lino – Chimwendo Banda

Rabson Kondowe

Zokonzekera za Misa yapadera yokumbukira malemu Dr Chilima zili mkati

Steve Dakalira
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.