M’modzi mwa adindo ku unduna woona za madzi ndi zaukhondo, a Alexander Mwangonde, ati dziko la Malawi silikuchita bwino pa nkhani zaukhondo, zimene zikupereka chiopysezo ku matenda.
A Mwangonde anati matendawa ndi monga kolera komanso ena.
Iwo anati mwa mabanja 100 aliwonse, mabanja 49 okha ndi amene amakwanitsa kutsatira njira zoyenera zaukhondo monga kusamba m’manja pafupipafupi komanso kusamala zinyalala.
A Mwangonde amayankhula izi pa kanema wa wayilesi ya boma ya MBC munzinda wa Lilongwe pa mtsutso okhudza nkhani zaukhondo umene anthu osiyanasiyana, kuphatikizapo mafumu, akatswiri a zakafukufuku, akuluakulu a ku unduna wa zaumoyo komanso nzika, amakambirana momwe angathetsere mavutowa.
Mtsutsowu unakonzedwa ngati njira imodzi yofalitsira uthenga olimbikitsa anthu onse m’dziko muno kuti adziyika chidwi pankhani zaukhondo.
Nduna ya za madzi ndi ukhondo, a Abida Mia, anatsegulira sabata yolimbikitsa ukhondo pa 21 October chaka chino.