Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Boma lasintha alembi ena muma unduna

Boma lasintha alembi ena muma unduna
Boma lasintha maundindo a alembi akulu a maunduna ena.
M’neneri mu ofesi ya mlembi wa mtsogoleri wa dziko lino ndi nduna zake, a Robert Kalindiza, atsimikiza za nkhaniyi.
Ena mwa anthu amene asinthidwa ndi awa: a Chikumbutso Mtumodzi amene anali m’modzi mwa akuluakulu ku unduna wazofalitsa nkhani pano ndi mlembi wamkulu ku unduna wa zachinyamata, a Hetherwick Njati amene anali mlembi wamkulu ku unduna wazofalitsa nkhani pano apita ku unduna wazachuma, a Chikondano Mussa amene anali mlembi wamkulu ku unduna wa zamaphunziro pano ndi mlembi wamkulu ku unduna owona za ogwira ntchito.
A Kalindiza ati kusinthaku sikwachilendo ndipo kukugwirizana ndi masomphenya a mtsogoleri wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera owonetsetsa kuti maunduna akugwira ntchito mokomera a Malawi.

Related posts

Tidzagwira ntchito mwaukadaulo pa chisankho cha 2025, watero mkulu wa MBC

Alinafe Mlamba

Wapereka mimba kwa mwana wobereka yekha

Rabson Kondowe

Kusowa kwa chakudya kwakula m’chigawo cha SADC

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.