Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Kulowetsa galimoto mozemba ndi mlandu

Bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority MRA lati likukumana ndi mavuto pa ntchito yotolera misonkho, maka pa galimoto zimene zimalowa m’dziko muno mozemba.

Mkulu wazamalonda ku bungweli, a Wilma Chalulu, wati anthu ena samafuna kuti galimoto zawo azifufuze ngati analipira msonkho kapena ayi polowa m’dziko muno.

A Chalulu apempha olembankhani kuti athandize kudziwitsa anthu zakufunika kopereka msonkho pa galimoto polowa mdziko muno komanso kupereka mpata ku bungweli kugwira ntchito mosavuta yofufuza galimoto zamtunduwu.

Boma limagwiritsa misonkho munjira zosiyanasiyana monga kumanga misewu, sukulu, zipatala, nyumba za ogwira ntchito m’boma komanso kupereka malipiro awo.

 

Related posts

Chakwera wafika m’dziko la UAE

Romeo Umali

Akupha makwacha ndi bizinesi ya tiyi lumu ku Lilongwe

MBC Online

Mlimi apata mphoto ya K10 million

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.