Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local News

Boma, asodzi agwirana manja pofuna kuchulukitsa nsomba m’nyanja ya Malawi

Nthambi yoona za usodzi yachita mgwirizano ndi mabungwe a asodzi ang’onong’ono m’maboma a Nkhatabay ndi Nkhotakota pofuna kuwapatsa mphamvu ndi umwini poteteza nsomba mu nyanja ya Malawi.

Mkulu oona za usodzi m’dziko muno, Hastings Zidana, ati mgwirizanowu uthandiza kuti nsomba zichuluke mu nyanjayi komanso pakufunika ndondomeko zoyoyenera mu gawo la usodzi.

Malinga ndi a Zidana, nyanja ya Malawi ikutulutsa nsomba zokwana matani 180,000, zomwe ndi zoyandikana ndi masomphenya a boma pofuna kukwanitsa kuti chiwerengerochi chikwane 350,000 metric tonnes pofika chaka cha 2030.

Mkulu wa bungwe la Ripple Africa, a Force Ngwira, ati iwo apitiriza kugwira ntchito zosiyanasiyana zokhudza usodzi mpaka anthu atasintha kaganizidwe ndikuyamba kusamala nsombazi.

 

Related posts

Parish ya Nzama yakwana zaka 125

Romeo Umali

Malawian Artists set to shine at Jamaica’s Reggae Month

MBC Online

‎Relegated Hammers turn pain into power in Castel Cup run

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.