Malawi Broadcasting Corporation
Local News

A Chakwera akutsogolera aMalawi pa mapemphero okumbukira ufulu wa dziko lino

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero akutsogolera mtundu wa aMalawi pa mapemphero apadera okondwelera kuti dziko la Malawi lakwanitsa zaka 60 pa ufulu odzilamulira.

Pamwambowu palinso wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Michael Usi, atsogoleri a mipingo yosiyana, nduna za boma ndi akazembe amaiko ndi mabungwe osiyanasiyana.

A Chakwera ndi amene adalamula kuti chaka chino pasakhale zochitikachitika monga zimakhalira nthawi zonse koma mapemphero okha chifukwa cha ziphinjo zomwe dziko lino lakumana nazo, kuphatikizapo imfa ya amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu.

Pa mwambowu, omwe ukuchitikira ku BICC mu mnzinda wa Lilongwe, anthu anakhala chete mphindi imodzi pokumbukira ndikupereka ulemu kwa malemu Dr Saulos Chilima ndi ena asanu ndi atatu.

Mutu wa Mapempherowa ndi ‘Kuyenda limodzi mochilimika’.

 

Olemba Isaac Jali

Related posts

Bad Start for Malawi’s Gomes at Paris

Romeo Umali

Airtel Malawi enhances security to combat mobile money fraud

Rabson Kondowe

TNM Mpamba launches innovative service for Malawians in Israel to send money home

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.