Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Awanjata pogulitsa mankhwala owopsa

Anthu asanu ndi awiri awatsekera ku polisi ya Ntcheu atawagwira akugulitsa mankhwala owopsa ophera tizilombo monga anankafumbwe mopanda chiloleza m’misika m’bomali.

Mmodzi wa akuluakulu ku bungwe la Pesticides Control Board, a Benson Kaphandira, ati mankhwalawa omwe ndi amapilisi komanso ena amadzi, ndi owopsa kotero kuti akuvulaza komanso kupha anthu ochuluka.

Mneneri wa apolisi ku Ntcheu, a Jacob Khembo, ati anthu  omwe awamangawa, akuyankha milandu yogulitsa mankhwala owopsa popanda chilolezo komanso kugulitsa mankhwala osavomerezeka.

Iwo ati ntchitoyi ipitilira pothana ndi mchitidwewu.

Related posts

DHRMD to digitalise all personal files in public service

Romeo Umali

International Blantyre Cancer Centre Inaugurated

Secret Segula

Chakwera to visit Vatican, Germany

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.