Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Awamanga powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende

Apolisi ku Zomba amanga Estery Evance wazaka 19 ndi Bonface Phiri wazaka 22 powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende yaikulu ya Zomba.

Ofalitsankhani wapolisi ku Zomba, Patricia Sipiliano, wati Phiri, yemwe ali pa limande ku ndende ya Zomba, anakaonekera ku khoti pa mlandu womwe anapalamula m’mbuyomu.

Pomwe Phiri amabwelera ku ndende, Evance anatenga nsapato zomwe zimadziwika kuti Gwaladi ndikupereka kwa mzakeyo ndipo oyang’anira ndende anadabwa ndi izi.

Iwo atayang’ana pansi pa nsapatozo pomwe panali pong’ambika, anapeza kuti kwabisidwa fodya wamkulu. Atawafunsa, anlephera kufotokoza zomveka.

 

Related posts

Ntchito za ICT ndi zandalama — Kunkuyu

Romeo Umali

ActionAid hands 12 motorcycles to health project partners

Rabson Kondowe

Illovo hands over K100 Million to Chikwawa District Council for cyclone survivors’ housing project

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.