Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

APOLISI KU LIMBE ALONJEZA KUPEREKA CHITETEZO CHOKWANIRA

Mkulu watsopano wa Polisi ya Limbe, a Edwin Mkhambo, watsimikizira anthu ochita malonda mderali komanso madera ozungulira kuti aonetsetsa kuti kuli chitetezo chokwanira.

A Mkhambo anena izi pa msonkhano wa atolankhani komwe anatsindika kuti ntchito yoika ma camera othandizira kukhwimitsa chitetezo (CCTV camera pachingerezi), ikuthandiza kwambiri.

A Mkhambo alowa mmalo mwa a Gladwell Chipumphula, amene pano ndi wachiwiri kwa komishanala wa apolisi kuchigawo cha kummawa.

WOLEMBA: GHWABUPI ANGELA MWABUNGULU

Related posts

CHUMA CHA MALAWI CHIKWERA NDI 3.3 PERCENT CHAKA CHINO – IMF

Blessings Kanache

Amangidwa poganiziridwa kuti anaba katundu wa ofesi

Mayeso Chikhadzula

NEEF yati sikupereka ndalama za ulere

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.