Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

Zinthu zambiri zasintha — Chithyola Banda

 

Nduna yoona zachuma, a Simplex Chithyola Banda, ati zinthu zambiri zasintha ndipo chuma chayamba kubwelera m’chimake.

Iwo amayankhapo pa lipoti la bungwe la Afrobarometer limene kafukufuku wake anachitika chaka chatha koma latulutsidwa mwezi uno.

Lipotili lati panthawi yomwe ankapanga kafukufuku, a Malawi ambiri anawonetsa kusakondwa ndi m’mene chuma chinkayendera panthawiyo.

Koma a Chithyola Banda ati pofika pano, zambiri zasintha.

Iwo ati mwachitsanzo, vuto la mafuta linatha, mitengo yachakudya ikutsika, mayiko ndi mabungwe ayambiranso kuthandiza dziko lino komanso kusowa kwa ndalama zakunja kwachepa.

Ndunayi yawonjezeranso kuti zinthu zipitilira kuchita bwino pansi pa ndondomeko ya zachuma imene aphungu akuyikambirana.

“Ndikuwalimbikitsa kuti adzachitenso kafukufuku wina miyezi itatu ikubwerayi, adzapeza zotsatira zosiyana kamba koti zinthu zikusintha tsopano,” a Chithyola Banda anatero.

 

Related posts

Lilongwe Immigration Office resumes passport printing

Romeo Umali

TNM UNVEILS AGULU BUNDLE FOR YOUNG AND FREE

MBC Online

VICTORY AGAINST CORRUPTION IS CLOSE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.