Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi agwira akuba amenenso anagwililira ophunzira ku Domasi Institute College

Apolisi ku Zomba amanga a Jaru Kambanga, 36 ndi a Patrick Bwanali, 31 powaganizira kuti anagwililira komanso kuba katundu wina pa malo ogona atsikana a sukulu ya ukachenjede ya Domasi Institute.

A Patricia Sipiliano, amene ndi ofalitsankhani wa Polisi ya Zomba, ati awiriwa pamodzi ndi enanso awiri omwe sakupezeka, adatchola ndi kulowa m’zipindazo atanyamula zida zochititsa mantha kenako anaba katundu wambiri, kuphatikizapo ma foni ndi zikwama.

A Sipiliano anaonjezerapo kuti atamaliza kubako, anthuwa anagwililira atsikana ena kenako anathawa.

 

Related posts

Five countries assist Malawi with 19,000 tonnes of grain

Romeo Umali

Mw geared to end Cholera by 2030

Romeo Umali

DAPP to intensify HIV Testing

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.