Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi agwira akuba amenenso anagwililira ophunzira ku Domasi Institute College

Apolisi ku Zomba amanga a Jaru Kambanga, 36 ndi a Patrick Bwanali, 31 powaganizira kuti anagwililira komanso kuba katundu wina pa malo ogona atsikana a sukulu ya ukachenjede ya Domasi Institute.

A Patricia Sipiliano, amene ndi ofalitsankhani wa Polisi ya Zomba, ati awiriwa pamodzi ndi enanso awiri omwe sakupezeka, adatchola ndi kulowa m’zipindazo atanyamula zida zochititsa mantha kenako anaba katundu wambiri, kuphatikizapo ma foni ndi zikwama.

A Sipiliano anaonjezerapo kuti atamaliza kubako, anthuwa anagwililira atsikana ena kenako anathawa.

 

Related posts

Umthetho Cultural Festival gets underway

Alinafe Mlamba

Social cash transfer beneficiaries hail Programme

Rabson Kondowe

Joggers On the Move to raise funds for Matekenya Health Centre in Dowa

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.