Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Apolisi abalalitsa anthu omwe amachita zipolowe pa mpingo wa CCAP wa Mibawa ku Mbayani

Apolisi aponya utsi okhetsa misonzi pobalalitsa anthu omwe anayambitsa zipolowe ku tchalitchi ya mpingo wa CCAP ya M’bawa ku Mbayani mu mzinda wa Blantyre.

Izi zinachitika potsatira kusamvana komwe kunabuka pakati pa akuluakulu a mpingowu ndi achibale a munthu wina yemwe wamwalira koma akuti anali membala wa mpingowu.

Malingana ndi mkulu owona zachitetezo ku bungwe la MBC yemwe anawona izi zikuchitika, a Ekaby Chikaphupha, malipoti akusonyeza kuti nkanganowu unabuka pomwe akuluakulu a mpingo anakana kuti sayimbira maliro a malemuwo ngakhale ali mkhristu wawo chifukwa chakhalidwe lake lopapira mowa mwa uchidwakwa.

Izi zinadzetsa mkwiyo kwa achibale amalemuyu komanso ena omwe amakhala mozungulira derali, zomwe zinapangitsa kuti ayambitse chipwilikiti poyamba kugenda komanso kufuna kutentha tchalitchili chifukwa chokana mkhristu wawo.

Powona izi, mpamene akuluakulu ampingowo anayimbira lamya apolisi ya Mbayani omwe anathamanga ndikudzaponya utsi okhetsa misonzi pofuna kubalalitsa anthu omwe amatsogolera zipolowezi.

Padakali pano,akuluakulu a mpingo wa CCAP wa Mibawa sanathilirepo ndemanga pa nkhaniyi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Death toll rises to four in Mzuzu road accident

Rudovicko Nyirenda

FCB BB beat Silver Strikers in NBS Charity Shield

MBC Online

Thyolo launches K598m school project

Chisomo Break
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.