Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

APM wabwera kumudzi

Prezidenti wakale wadziko lino, Professor Peter Mutharika, wabwerera kuno kumudzi lero masanawa.

A Mutharika, omwenso ndi mtsogoleri wachipani chotsutsa cha Democratic Progressive, afika kuno kumudzi kudzera kubwalo landege la Chileka munzinda wa Blantyre.

Poyambirira, akuluakulu a chipanichi adatsutsa zoti a Mutharika ali m’dziko la South Africa pomwe wayilesi ya MBC idafotokoza zakuchoka kwa mtsogoleriyu.

Mmneneri wachipani cha DPP, a Shadreck Namalomba, adakanitsitsa zoti a Mutharika achoka m’dziko muno kufikira pomwe mlembi wamkulu wachipanichi, a Peter Mukhito, anatulutsa kalata yovomereza kuti a Mutharika alidi kunja kwa dziko lino.

Panali mphekesera yoti a Mutharika amalandira thandizo la mankhwala m’dziko la South Africa ngakhale kuti chipanichi chimati apita kukagwira ntchito zina.

A Mutharika, omwe ali ndi zaka 86, akhala m’dziko la South Africa kwa sabata ziwiri.

Related posts

Piksy gears up for new album

Romeo Umali

KB soldiers killed by two bullets

Romeo Umali

‘My life is at risk’: Living with epilepsy in Malawi

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.