Malawi Broadcasting Corporation
News

Anthu 1,200 alandira matumba achimanga ku Balaka

Mtsogoleri wa Mpingo wa Salvation for All Ministries International, m’busa Clifford Kawinga, wapempha mabungwe ndi amipingo kuti agwirane manja pothandiza anthu omwe akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

A Kawinga anena izi pamene amagawa matumba achimanga kwa anthu 1,200 komanso kulalikira uthenga wa Mulungu m’dera la mfumu yaikulu Matola m’boma la Balaka.

M’busayu wati apitiliza kutumikira anthu powalalikira komanso kuthandiza zosowa zawo za thupi.

Iwo anagawanso ma Baibulo kwa mafumu ndi atsogoleri osiyanasiyana.

 

Wolemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Trust my capabilities — Daud

Rabson Kondowe

Hilal Africa reaches out to Mzuzu Muslim communities during Eid Al Adha

Alinafe Mlamba

Chess Lover Introduces Game to Malawi’s Prisons, Schools and Street Kids

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.