Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ansembe ndi akhristu akonzeka kulandira thupi la Dr Chilima ku St. Patrick’s Parish

Ku St Patrick’s Parish, zonse zokonzekera kulandira thupi la Dr Saulos Chilima zatha.

Padakalipano, anthu ochuluka afika kudzakhala nawo pa misa ya maliro a wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu.

Malemu Dr Chilima anali mkhristu wa mphamvu wa mpingo wa Katolika wapa Parish ya St Patrick’s ku Area 18.

Ndipo mwa zina, iwo anathandiza nawo pa ntchito yomanga tchalitchi chatsopano cha St Patrick’s.

President wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kutsogolera ulendo onyamula thupi ku Goodwill Funeral Services ku Area 4 mu mzinda wa Lilongwe kufika ku St. Patrick’s Parish ku Area 18.

 

By Isaac Jali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

FISH FARMING CATALYST TO ECONOMIC EMPOWERMENT

MBC Online

Amai atatu ali mchitokosi pamulandu wakuba ku Mangochi

Davie Umar

Olembankhani ndi mlatho wazochitika ku nyumba ya malamulo — CSAT

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.