Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ansembe ndi akhristu akonzeka kulandira thupi la Dr Chilima ku St. Patrick’s Parish

Ku St Patrick’s Parish, zonse zokonzekera kulandira thupi la Dr Saulos Chilima zatha.

Padakalipano, anthu ochuluka afika kudzakhala nawo pa misa ya maliro a wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu.

Malemu Dr Chilima anali mkhristu wa mphamvu wa mpingo wa Katolika wapa Parish ya St Patrick’s ku Area 18.

Ndipo mwa zina, iwo anathandiza nawo pa ntchito yomanga tchalitchi chatsopano cha St Patrick’s.

President wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kutsogolera ulendo onyamula thupi ku Goodwill Funeral Services ku Area 4 mu mzinda wa Lilongwe kufika ku St. Patrick’s Parish ku Area 18.

 

By Isaac Jali

Related posts

Apostle Kawinga agawa chimanga, mabaibulo Ku Mchinji

Yamikani Simtowe

LCC urges contractors to produce standard work

Romeo Umali

Alexander ‘Cage’ Likande wamwalira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.