Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Akumuganizira kuti wapha bwenzi lake

Apolisi ku Chiradzulu akufunafuna Steven Museu pomuganizira kuti wapha bwenzi lake lazaka 40, Bertha Nkolimbo.

Izi zachitika mmudzi wa Liphuthu, mfumu yaikulu Nkalo m’boma lomwelo la Chiradzulu. Ofalitsankhani wapolisi ku Chiradzulu, Cosmas Kagulo, wati malemuwo anachoka pa 17 June kupita kokamwa mowa koma sanabwelerenso.

Asanasowe, anthu ena anati anamuona Bertha ali kunyumba kwa Museu. Ndipo tsiku lotsatira, woganiziridwayo anatenga nsapato za malemuyo kukasiya ku malo omwera mowa ndikuuza mwini malowo kuti adzamupatsire nsapatozo Bertha kenako Museu sanaonekenso mmudzimo mpaka pano.

Anthu omwe anapita kukakumba manda mmudzimo ndiwo apeza thupi la malemuwo koma litawonongeka. Ndipo zotsatira za chipatala zawonetsa kuti malemu Bertha wafa atavulala mmutu.

Related posts

BANKING AMENDMENT BILL NEEDS FURTHER CONSULTATIONS

MBC Online

Gwengwe challenges maximisation of SVTP

Rabson Kondowe

TEVETA ILIMBIKITSA ACHINYAMATA OMWE ADASIYIRA SUKULU PA NJIRA KULIMBIKIRA NTCHITO ZALUSO

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.