Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local News Nkhani

Achinyamata awapempha kuti athandize boma pa chitukuko

Bungwe la Chiwalo Youth Network lalangiza achinyamata a m’boma la Phalombe kuti athandize kulimbikitsa ukhondo m’makomo mwawo komanso m’malo a boma monga ku Polisi ndi ku chipatala.

Wapampando wa bungweli, a Patrick Makwale, ndi amene ananena izi pamene achinyamata ena amagwira ntchito yosesa pa chipatala cha boma cha Nambazo komanso Polisi ya Nambazo m’bomalo.

A Makwale anati ndi okondwa poona kuti achinyamata ambiri ku Phalombe akuonetsa chidwi pa ntchiito za chitukuko, potukula miyoyo yawo komanso ntchito za boma.

 

Related posts

Suspects for Central Poultry Limited robbery netted

Alinafe Mlamba

Minister Hara calls for innovation within construction industry

Rabson Kondowe

600 households to receive seed money for business growth

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.