Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local News Nkhani

Achinyamata awapempha kuti athandize boma pa chitukuko

Bungwe la Chiwalo Youth Network lalangiza achinyamata a m’boma la Phalombe kuti athandize kulimbikitsa ukhondo m’makomo mwawo komanso m’malo a boma monga ku Polisi ndi ku chipatala.

Wapampando wa bungweli, a Patrick Makwale, ndi amene ananena izi pamene achinyamata ena amagwira ntchito yosesa pa chipatala cha boma cha Nambazo komanso Polisi ya Nambazo m’bomalo.

A Makwale anati ndi okondwa poona kuti achinyamata ambiri ku Phalombe akuonetsa chidwi pa ntchiito za chitukuko, potukula miyoyo yawo komanso ntchito za boma.

 

Related posts

Adzudzula mmodzi mwa atsogoleri a DPP kaamba kolankhula moopseza

Rabson Kondowe

First Lady’s Shaping the Future Foundation Hosts Fundraising Dinner at Kamuzu Palace

Alinafe Mlamba

UNGA UNDERWAY

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.