Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

Ana opyola 1,000 asiyira sukulu panjira ku Lilongwe m’miyezi ya April mpaka June

Ana pafupifupi 1, 200 asiyira sukulu pa njira munzinda wa Lilongwe pakati pa miyezi ya April ndi June chaka chino chokha chifukwa cha umphawi komanso kuwachitira nkhanza, khonsolo ya mzindawu yatsimikiza.

M’modzi mwa akuluakulu a khonsoloyi, a Derrick Mwenda, ndi amene anena izi pa msonkhano okumbukira mwana wamu Africa kwa mfumu yayikulu Kabudula m’boma la Lilongwe.

Ndipo wa pampando wa khonsolo yomweyi, a Dominick Banda, anadzudzula m’chitidwe omwe sukulu zina zikuchita owumiriza ophunzira kupereka ndalama zapadera, zomwe ati zikukolezera kuti ana asiyire sukulu panjira.

A Chrissie Mbundungu omwe ndi m’modzi mwa adindo a bungwe la Organization for Sustainable Socio-Economic Development Initiative, ati bungwe lawo ndi lodzipereka kuonetsetsa kuti ufulu wa maphunziro ukufikira ana onse m’Malawi.

 

Related posts

Zokonzekera za mwambo wa mapemphero okumbukira ufulu wa dziko lino zili mchimake

Rabson Kondowe

Zokonzekera gawo lachiwiri lokonza sikimu ya Mlambe zili mchimake

Romeo Umali

Ministry of Education for accelerated inclusive education

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.