Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News

ACB yamanga anthu asanu ndi atatu ku Immigration

Bungwe lothana ndi ziphuphu komanso katangale la ACB latsimikiza kuti lamanga anthu asanu ndi m’modzi powaganizira kuti amachita zachinyengo pa ntchito yodinda ziphaso ku nthambi ya Immigration.

Ofalitsankhani ku ACB, a Egrita Ndala, ati anthuwa awamanga kuti akayankhe mafunso okhudza m’chitidwe wa ziphuphu komanso katangale.

“Zoonadi tamanga anthuwa potsatira madandaulo a anthu komanso kafukufuku wachinsinsi yemwe tinachita okhudza zachinyengo kunthambiyi, ” anatero a Ndala.

Anayi mwa anthuwa ndi ogwira ntchito ku Immigration ndipo awiri enawo samagwira ntchito kumeneko.

 

Related posts

Chakwera calls for integrity

MBC Online

Judge for collective effort in promoting Human Rights, access to justice

Romeo Umali

Onesimus achenjeza akonzi a Ku Mingoli Bash

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.