Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News

ACB yamanga anthu asanu ndi atatu ku Immigration

Bungwe lothana ndi ziphuphu komanso katangale la ACB latsimikiza kuti lamanga anthu asanu ndi m’modzi powaganizira kuti amachita zachinyengo pa ntchito yodinda ziphaso ku nthambi ya Immigration.

Ofalitsankhani ku ACB, a Egrita Ndala, ati anthuwa awamanga kuti akayankhe mafunso okhudza m’chitidwe wa ziphuphu komanso katangale.

“Zoonadi tamanga anthuwa potsatira madandaulo a anthu komanso kafukufuku wachinsinsi yemwe tinachita okhudza zachinyengo kunthambiyi, ” anatero a Ndala.

Anayi mwa anthuwa ndi ogwira ntchito ku Immigration ndipo awiri enawo samagwira ntchito kumeneko.

 

Related posts

Onani to contest for MCP Director of Youth

Romeo Umali

Institutions providing poor quality food to children — Committee

Romeo Umali

Dedza District Council calls off council meeting

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.