Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Kusayendetsa bwino chuma ku Netball kuopseza othandiza — NAM

Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa manja m’dziko muno la NAM lati kukanika kuyendetsa bwino chuma kumasewerowa kukuthamangitsa kampani zimene zili ndi kuthekera kokweza masewerowa.

Mlembi wa mkulu wa bungweli, a Yamikani Kauma, ndi amene ayankhula izi munzinda wa Lilongwe pa maphunziro a zachuma amene anakonza ndi a Old Mutual, omwe amathandiza masewerowa m’chigawo chapakati kudzera ku kampani yawo yotchedwa MPICO.

A Patricia Chatsika, m’modzi mwa akuluakulu a ku Old Mutual, anati cholinga cha maphunzirowa ndi kuthandiza osewera komanso oyendetsa masewerowa m’mene angagwiritsire ntchito ndalama.

Osewera ndi oyendetsa masewero a Netball okwana 100 m’chigawo chapakati ndi amene achita nawo maphunzirowa.

 

Related posts

MIA TO LOBBY FOR CLEAN WATER AT UN 2023 WATER SUMMIT

MBC Online

One dead, 7000 displaced in KK floods

Rabson Kondowe

Rumphi CSOs push for increased women and youth participation in elections

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.