Malawi Broadcasting Corporation
Africa Crime Local News Nkhani

ABWEZA GALIMOTO  KWA MWINI

Khothi la Magistrate ku Blantyre lalamula apolisi komanso  a dipatimenti ya zankhalango kuti apereke  galimoto ya mtundu wa Scania yamatani 10 yomwe nambala yake ndi NN 10435 kwa mwini wake patapita nthawi galimotoyi ataigwira pa mulandu wokhudza kuononga zachilengedwe.

Galimotoyi  anaigwila apolisi pa 21 December 2023 pa roadblock ya Ngumbe akuyendetsa mwini wake Jonasi Billiat atanyamula matumba a makala.

Malinga ndi zomwe MBC yapeza mkulu wapolisi owona zotengera milandu kubwalo lamilandu omwe ndi  wachiwiri kwa komishonala, a Levison Mangani,  anapempha bwalo kuti lisapereke galimotoyi kaamba koti mwini wake ndi amenenso anapalamula mlanduwu popezeka akuyendetsa ponena kuti ndiye mbali ina ya umboni waukulu wa boma pa nkhaniyi.

Galimoto yomwe ili umboni pa mlanduwu.

Komabe magistrate amene akuunguza nkhaniyi wapereka galimotoyi kwa a Biliati omwe anakali pa belo yaku khothi pomvela zomwe  yemwe amawaimila anafotokozera bwaloli.

Kuyambila chaka chatha apolisi mogwilizana ndi a dipatimenti ya zankhalango komanso bungwe lolimbana ndi mchitidwe wa ziphuphu ndi katangale akhala akugwira ntchito yothana ndi mchitidwe wosakaza nkhalango pootcha makala.

Bwalo komanso anthu ena omwe akutsatila nkhaniyi  anakaona galimotoyo komanso matumba amakalawo kuma ofesi a zankhalango mu mzinda wa  Blantyre.

Bwalo la milandu likuyembekezeka kudzamva za nkhaniyi pa 8 February 2024.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

SADC SUMMIT ENDS – LEADERS PLEDGE ECONOMIC GROWTH

MBC Online

“Tisanaloze zala adindo tidziunike kaye ifeyo”

Paul Mlowoka

ULADI MUSSA ATHOKOZA DR CHAKWERA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.