Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Abusa apereka penti ku Polisi ya Chinsapo

Atsogoleri a mipingo ku Likuni ndi kwa Chinsapo ku Lilongwe apereka penti yokwana malita 35 ku Polisi ya Chinsapo Unit kuti akonzere denga limene liri ndi dzimbiri.

Mkulu wa Likuni and Chinsapo Pastors Fraternal, Reverend Daniel Masamba, anati zimakhala zomvetsa chisoni kuona apolisi akupulumutsa katundu wa nkhaninkhani kwambava koma kulephera kupulumutsa denga lawo.

Mkulu wa Polisiyi, a Mavuto Banda, anayamikira chifukwa cha mphatsozi.

M’mbuyomu, atsogoleri a mipingowa anabyzala mitengo pa Polisiyo kaamba kogwira bwino ntchito.

Olemba: Raymond Midaya

Related posts

Two remanded men charged with murder

Romeo Umali

Chakwera calls for order in the mining sector

Romeo Umali

PREMIER BET DISPELS CLOSURE RUMOURS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.