Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Abusa apereka penti ku Polisi ya Chinsapo

Atsogoleri a mipingo ku Likuni ndi kwa Chinsapo ku Lilongwe apereka penti yokwana malita 35 ku Polisi ya Chinsapo Unit kuti akonzere denga limene liri ndi dzimbiri.

Mkulu wa Likuni and Chinsapo Pastors Fraternal, Reverend Daniel Masamba, anati zimakhala zomvetsa chisoni kuona apolisi akupulumutsa katundu wa nkhaninkhani kwambava koma kulephera kupulumutsa denga lawo.

Mkulu wa Polisiyi, a Mavuto Banda, anayamikira chifukwa cha mphatsozi.

M’mbuyomu, atsogoleri a mipingowa anabyzala mitengo pa Polisiyo kaamba kogwira bwino ntchito.

Olemba: Raymond Midaya

Related posts

Save the Children pledges support as Malawi launches National Children’s Commission

McDonald Chiwayula

THE DEAD AND NEGLECTED DAMS OF BLANTYRE

MBC Online

Bambo alamulidwa agwire jere kwa zaka 12 atagwilira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.