Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News Nkhani

Abambo 41 pa 100 sadziwa kuti ali ndi HIV — NAC

Bungwe la National Aids Commission (NAC) lati abambo 41 pa 100 alionse m’dziko muno samadziwa kuti ali ndi kachirombo Ka HIV komwe kamayambitsa matenda a AIDS.

A Francis Mabedi, omwe ndi m’modzi mwa akuluakulu ku bungwe la NAC, ati izi zili chomwechi kaamba ka kuti abambo ambiri amaopa kupita ku chipatala, zomwe ati ndi zosayenera.

“Abambo ambiri sakhala ndi chidwi chopita ku chipatala kuyerekeza ndi amayi. Nthawi zambiri amachita mantha,” a Mabedi anauza atolankhani mumzinda wa Blantyre.

Atolankhani kumvetsera mwa chidwi.

Malinga ndi kafukufuku wa za umoyo, anthu 1 million ndi amene ali ndi HIV m’dziko muno.

Olemba: Mercy Zamawa

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Jalira Girls Secondary School to broaden girls’ dreams

MBC Online

Major Aidini laid to rest

Davie Umar

ZAMBIRI MWA ZIMENE A CHAKWERA ANALONJEZA MU SONA YA 2023 ZACHITIKA – NDUNA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.