Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Chilima adatukula kampani yathu ya Airtel — Kamoto

Mkulu wa kampani ya Airtel Malawi, Charles Kamoto, wati malemu Dr Saulos Chilima anali munthu wodzipereka ndi wokonda ntchito.

Poyankhula ndi MBC, a Kamoto ati kampani ya Airtel Malawi sidzaiwala zazikulu zomwe adachita posintha kagwilidwe ka ntchito kumpaniyi.

“Ma tower ambiri omwe mukuwaona m’dziko muno a Airtel, malemu a Chilima ndi omwe adathandizira kuti ayike malo osiyanasiyana,” anatero a  Kamoto.

Iwo anati adaphunzira zinthu zambiri kuchokera kwa malemu Dr Chilima.

Malemu Dr Chilima adagwilako ntchito ku kampani zosiyanasiyana m’dziko muno, kuphatizapo Airtel Malawi, asadayambe kuchita za ndale.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Nkhonya ya Hannock Phiri ndi Regene Champion ikununkhira

Foster Maulidi

Karonga, Chitipa signs development deal with Lotus Africa

Rudovicko Nyirenda

Sports Council partners MBC for minority sports popularisation

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.