Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘A Chakwera ataya kholo mu uzimu’

Mlangizi wa prezidenti pa ndale a Kingsley Sulamoyo ati mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wataya kholo mu uzimu pa imfa ya the Very Reverend Killion Mgawi.

A Sulamoyo, omwe ayankhula mmalo mwa Dr Chakwera, ati panthawi yomwe mtsogoleri wa dziko linoyu anali pa sukulu ya ubusa, anakhala limodzi ndi abusa a Mgawi ndipo amawalangiza ndi kuwaunikira m’magawo osiyanasiyanasiyana.

A Sulamoyo ati Dr Chakwera ndiothokoza kuti abusa a Mgawi asiya anthu odalirika omwe akugwira ntchito zikuluzukulu mothandizana ndi a Prezidenti kuyendetsa dziko lino.

Iwo apempha a Malawi kuti aphunzire pa momwe abusa a Mgawi akhalira moyo wawo pa dziko pano.

Mtsogoleri wa dziko lino wapepesa banja la a Mgawi pa imfayi ndi ndalama yokwana K2 million.

Related posts

‘Lekani kusala ndi kuchitira nkhanza anthu omwe ali khungu lachi alubino’

Rabson Kondowe

Mwambo wa Kulamba ulipo chaka chino

McDonald Chiwayula

‘Tiganizireni poonjezera ndalama za mtukula pakhomo’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.