Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

MPUNGWEPUNGWE KUNYUMBA YAMALAMULO

Kuli mpungwepungwe ku nyumba ya malamulo pomwe zokambirana kunyumbayi zayamba ndipo a Kondwani Nankhumwa komanso  a Mary Navicha  anaimilira ngati mtsogoleri wa zipani zotsutsa.

Awiriwa anaimilira Sipikala wanyumbayi atafunsa kuti Otsutsa boma ayankhepo pa zomwe anakambirana ku komiti ya atsogoleri oyendetsa zokambirana za nyumba yamalamulo.

Kusamvana kunabuka mnyumbayi  pomwe Sipikala wanyumbayi a Catherine Gotani Hara anavomereza a Kondwani Nankhumwa ngati mtsogoleri wa otsutsa ponena kuti malingana ndi chiletso cha khothi Pakadali pano a Mary Navicha sangaimilire mbali yotsutsayi komanso ku sanali nawo pazokambiranazi.

Apa mpomwe akumbali yotsutsa a chipani cha DPP anaima kutsutsana ndi gamulo la sipika.

A Gotani Hara alamula a Navicha ndi a Nankhumwa kuti akhale pansi kutengera ndi malamulo a mnyumbayi.

Pakadali pano zokambira nyumba yi aziimitsa kaye kwa mphindi khumi.

 

Wolemba: Olive Phiri ndi  Beatrice Mwape

Related posts

Chakwera extends Ramadan wishes to Muslim community

Alinafe Mlamba

AMEA POWER TO INSTALL 50 MEGAWATTS FACILITY

MBC Online

Former Nkhoma Synod Secretary General inaugurated as Group Gusu

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.