Malawi Broadcasting Corporation
Africa Local News Nkhani Politics

A CHAPONDA ALI PA MSONKHANO WINA NGATI WACHIWIRI KWA MTSOGOLERI WA DPP

Phungu wa nyumba yamalamulo wadera la kuzambwe kwa boma la Mulanje, a George Chaponda, amene awathamangitsa ku msonkhano wa akuluakulu a ku nyumba ya Malamulo komwe amafuna kukaimira ngati mtsogoleri wa aphungu otsutsa pa zokambiranazo, tsopano ali ku msonkhano wa bungwe la Democracy Works Foundation komwe akuimiranso chipani cha DPP.

Bungwe la Democracy Foundation lakonza maphunzirowa pofuna kupereka upangiri kwa akuluakulu a zipani zisanu ndi chimodzi zimene zili ndi aphungu mu nyumba ya malamulo pa zomwe akuyenera kuchita ndi kutsata pa ndondomeko yaza chuma yomwe aikambirane ku nyumba ya malamulo.

Poyankhula pozizindikiritsa, a Chaponda auza msonkhanowu kuti iwo ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha DPP mchigawo chakummwera.

Iwo awathamangitsa ku msonkhano oyambawo kumene akuluakulu a ku nyumba ya malamulo akukambirana mmene mkumano wa nyumba ya Malamulo, umene uyambe lachisanu, uyendere.

Wolemba: Beatrice Mwape

Related posts

60,000 illegal fishing gear destroyed in Nkhata Bay

MBC Online

Farmers regain hope in Mutharika’s first 100 days

Rabson Kondowe

‘Malamulo a chipani akuvomereza atosgoleri ake kudzachita mgwirizano ndizipani zina’

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.