Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndife okondwa kuti boma limatiika mmapulani ake – Ras Mwanamanga

Wachiwiri kwa nduna yaza ulimi Benedicto Chambo anacheza ndi akuluakulu achipembezo chachi Rasta munzinda wa Lilongwe.

A Chambo, omwenso ndi phungu wadera la Mangochi – Makanjira, ati ma rasta ndi anthu ofunikira kwambiri pa chitukuko cha dziko lino choncho akufunika osamawssiya mmbuyo pokwaniritsa masomphenya a Malawi 2063.

Iwo ati ichi ndichifukwa chake mtsogoleri wa dziko lino amaonetsetsa kuti aliyense adzitha kukhala ndi mwayi okhala m’maudindo osiyanasiyana ofunikira.

Ras elder Mwanamanga, yemwenso ndi mmodzi mwa atsogoleri ku mpingo wachi Rasta Ku Nyabingi House ku Area 17 munzinda wa Lilongwe, wati ndi okondwa kuti boma layika padera mapologalamu osiyanasiyana omwe cholinga chake nkusintha miyoyo ya anthu m’dziko muno.

Lachisanu pomwe aphungu amamaliza msonkhano wawo, ma rasta anali nawo kunyumbayi kutsatira zokammbiranazi.

Related posts

MEC, NICE intensify election awareness campaign

Rabson Kondowe

Baka City FC registers first win in TNM Super League

Rabson Kondowe

Climate smart programme brings new life to degraded land in Likoma

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.