Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Save The Children yapereka mbaula zamakono ku Lilongwe

Mabanja okwana makumi asanu ammudzi mwa mfumu yaikulu Masumbakhunda ozungulira khalango ya Dzalanyama m’boma la Lilongwe ali ndi chimwemwe atalandira mbaula zamakono zoyendera mphamvu ya dzuwa kuchokera ku bungwe la Save the Children.

Malinga ndi m’modzi mwa akuluakulu ku bungwel, a Bright Chidzumeni, kupereka mbaulazi ndi njira imodzi yochepetsa mavuto owononga nkhalango ya Dzalanyama, mmene anthu akhala akudulamo mitengo mopanda chilorezo ndicholinga chopanga nkhuni komanso makala ophikira.

M’modzi mwa anthu amene alandira nawo mbaulazi, a Lydia Banda, anati ithandiza kuchepetsa mchitidwe ogwiritsa ntchito ana kukafuna nkhuni ku nkhalangoyi popeza mbaulazi zimagwiritsa ntchito nkhuni zochepa.

 

Related posts

Boma lati alimi atha kukolora zochuluka

Romeo Umali

Bullets sign Chitiyo

Romeo Umali

Dzatengeni ngongole za NEEF — Kabwila

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.