Malawi Broadcasting Corporation
Crime Nkhani

Mayi wathawa atatentha manja a mwana wake

Apolisi ku Mangochi akufunafuna mayi Gladys Lingoni amene wathawa pomuganizira kuti watentha manja a mwana wake wa zaka zisanu ndi chimodzi chifukwa anadya ndiwo za soya zomwe anakonza kuti adyere msima.

Ofalitsankhani za polisi ya Mangochi, Amina Tepani, Daudi wati Lingoni ndi wammudzi mwa Sadibwa mdera la mfumu yaikulu Mkanda m’boma la Mulanje.

Panopa apolisiwo akupempha anthu akufuna kwabwino omwe angadziwe komwe mayiyo wabisala kuti awadziwitse chifukwa wasiyanso ana ena pakhomo pake.

Olemba Davie Umar.

Related posts

Immigration ikufuna kukhala ya mphamvu pa masewero

Rabson Kondowe

Muli ndi ufulu olowa chipani chomwe mwafuna – Brown Mpinganjira

Rabson Kondowe

Inkosi M’mbelwa yadzudzula ndale zonyozana

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.