Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local News Nkhani Politics

Inkosi M’mbelwa yadzudzula ndale zonyozana

Inkosi ya Makhosi M’mbelwa V yati aMalawi akuyenera kupewa m’chitidwe wa ziwawa chifukwa dziko lino limakonda mtendere.

Inkosiyi imayankhula izi pa mwambo wa Umthetho ku Hora m’boma la Mzimba.

Mfumuyi inalangizanso zipani zonse za ndale ndi owatsatira, pamene masiku azisankho aluyandikira, kuti apewe ndale zonyozana chifukwa sizingamange dziko lino.

Mfumuyi inatinso iyi ndi nthawi yomwe aMalawi akuyenera kugwirana manja poonetsetsa kuti m’fundo zomwe boma linalonjeza zikukwaniritsidwa.

Olemba: Jackson Sichali

Related posts

Malawi ipindula ndi ntchito yotukula luso lazaumoyo

Romeo Umali

PHALOMBE REACHES 70 PERCENT POLIO VACCINE TARGET

MBC Online

Illovo Sugar launches Rise for Girls Programme

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.