Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local News Nkhani Politics

Inkosi M’mbelwa yadzudzula ndale zonyozana

Inkosi ya Makhosi M’mbelwa V yati aMalawi akuyenera kupewa m’chitidwe wa ziwawa chifukwa dziko lino limakonda mtendere.

Inkosiyi imayankhula izi pa mwambo wa Umthetho ku Hora m’boma la Mzimba.

Mfumuyi inalangizanso zipani zonse za ndale ndi owatsatira, pamene masiku azisankho aluyandikira, kuti apewe ndale zonyozana chifukwa sizingamange dziko lino.

Mfumuyi inatinso iyi ndi nthawi yomwe aMalawi akuyenera kugwirana manja poonetsetsa kuti m’fundo zomwe boma linalonjeza zikukwaniritsidwa.

Olemba: Jackson Sichali

Related posts

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Romeo Umali

Police arrest two over counterfeit maize flour

MBC Online

Health authorities denounce fake HIV cure rumours

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.