Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dr Usi ati alimbikitsa umodzi

Dr Micheal Usi, amene ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, ati achita zotheka polimbikitsa chipani cha UTM, monga mtsogoleri wachipanichi, kuti chikhale champhamvu.

Iwo ati cholinga chawo ndikukwaniritsa masomphenya a yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, malemu Dr Saulos Chilima.

Dr Usi anena izi pamene amacheza ndi anthu a kumudzi kwawo kwa Golden kwa mfumu yaikulu Chikumbu m’boma la Mulanje.

Iwo atsimikiziranso anthu a m’boma la Mulanje kuti boma ladzipereka potukula miyoyo yawo, kuphatikizapo kupereka ngongole kwa ochita bizinezi.

 

Related posts

UN, Malawi strengthen migration governance

Chisomo Break

SANGANAYI SOCIAL CLUB DONATES TO CYCLONE FREDDY SURVIVORS

MBC Online

Govt committed to transforming Malawi – Chimwendo Banda

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.